|
Apostles Creed
Study Guide in Chichewa
Phunziro la
Chikhulupiliro cha Apositoli mu Chichewa
Chikhulupiliro cha Apositoli
sinthambi ya baibulo, koma ndi uthenga wa maphunziro a tchalichi cha Akhrisitu.
Mawu adzibvomerezi khumi ndi ziwiri a choonadi analembedwa zaka mazana ndi
mazana apitawo, koma alibe ndi tathauzo lodzichepetsa, kuwala ndi choonadi.
Tiphunzira mawu onse ndi
ndime za m'baibulo ndi mafunso. Mungaphunzire mapeji otsatilawa pa nokha kapena
kuphunzila pokambilana mu magulu.
I. Ndikhulupilira Atate
Mulungu Mlengi wakumwamba ndi dziko lapansi.
1. Werengani nkhani ya
chilengedwe mu Genesesi ndime yoyamba ndi yachiwiri.
2. Werengani mau a Mulungu
kwa a Isilayeli muYesaya 40:6-31.
3. Werengani za m'mene
Mulungu anayakhira za makayiko a mwana wa Mulungu m'bukhu la Ntchito ndime
38-41.
4. Werengani m'mene Mulungu
aliri ndi anthu amene samamupembeza ngati mlengi m'bukhu la Aroma 1:18-25.
Mafunso:
1. Genesesi ndi bukhu
lotsabvuta, anthu achikhulupiliro chochepa angalimvetse. Nanga ndi chifukwa
chiyani anthu ena samabvomeleza nkhani ya chilengedwe? Werenganinso Akorinto
oyamba 1:18-31.
2. Poti Mulungu ndi wamkulu
wamphamvu, wodzidalira, ndi chifukwa chiyani amadandaula za anthu? Onaninso
bukhu la Petro oyamba 3:8-10.
3. Tikatenga bukhu la
Ntchito ngati chitsanzo cha maweluzo a chikhalidwe, tingagwirizane nadzo,
kapena kukambirana ndikufunsana, kapena kunyoza? Werengani Ntchito ndime
yoyamba ndi yachiwiri. Werenganinso 2:9-10.
4. Kodi ndi tchimo lanji
liri mu ndime imeneyi nanga Mulungu wachita chiyani?
Mayankho:
1.
_____________________________________________________
_______________________________________________________
2.
_____________________________________________________
________________________________________________________
3.
_____________________________________________________
_______________________________________________________
4.
_____________________________________________________
_______________________________________________________
II. Ndi mwa Yesu Khrisitu,
Mwana wake yekha, wa Atate athu.
1. Werengani m'mene kubadwa
kwa Yesu kunalembedwela m'bukhu la Luka 1:26-38 ndi m'mene anaukila kwa akufa
m'bukhu la Luka 2:1-20.
2. Werengani m'mene Yesu
anenera za chigwirizano chake ndi Mulungu Atate m'bukhu la Yohane 20:17
ndiponso
mavesi 28-29.
3. Werengani Aroma 8:1-4
kuti muone chikondi cha Mulungu Atate ndi Mwana wake Yesu Khrisitu.
4. Werengani Yohane 1:1-5
za ulemelero wakumwamba wa Yesu.
Mafunso:
1. Onani m'mene analembera
ndime ya Mika 5:2 zaka mazana apitawo Yesu asanabadwe ndi nkhani ya
m'chipangano chatsopano.
2. Ndi lonjezo lotani
limene Yesu analonjeza omubvomela ngati mpulumutsi ndi mtsogoleri wao?
3. Kodi vesi 3 limatiuza
bwanji kuti Yesu ndi ndani ndipo ndi chifukwa chiyani anabwera pa dziko
lapansi?
4. Nanga ndime imenenyi
imatiuza bwanji za kufana kwa Atate ndi Mwana?
Mayankho:
1.
_____________________________________________________
_______________________________________________________
2.
_____________________________________________________
________________________________________________________
3.
_____________________________________________________
_______________________________________________________
4.
_____________________________________________________
_______________________________________________________
III. Kudzera Mumzimu
Woyera, anabadwa kwa mai Maria.
1. Werengani zimene Mateyu
woyera ananena poonjezera nkhani ya Luka za kubadwa kwa Yesu mu Mateyu
1:18-25.
2. Werengani Ahebri 4:14-15
ndi Luka 2:41-52 m'mene Yesu anakhalira pa dziko lapansi ngati mwana wa
Mulungu.
3. Werengani Yesaya 9:6-7
ndi Yesaya 7:13-14 kuti muone zimene Chipangano Chakale chimanena zakubadwa
kwa Yesu ndi momwe zinaonekera mu Chipangano Chatsopano.
4. Werengani mavesi 17-23 a
Ayuda kuti muone mphamvu ya mzimu woyera my moyo wa Akhrisitu.
Mafunso:
1. Kodi Yosefe ankafuna
kutani atadzindikira kuti Maria ndiwodwala, nanaga anachita chiyani?
2. Muli ndi maganizo anji
podzindikira kuti Yesu ndi mtumiki wathu kwa Atate, ndiponso kuti anakhala
padziko lapansi ndimabvuto ngati a inu ndi ine.
3. Kodi ndi chifukwa
chiyani kubadwa kwa Yesu kudzera mu mzimu woyera kuli kofunika kwa Akhrisitu?
4. Nanga ngati Akhrisitu
tiyenera kutani?
Mayankho:
1.
_____________________________________________________
_______________________________________________________
2.
_____________________________________________________
________________________________________________________
3.
_____________________________________________________
_______________________________________________________
4.
_____________________________________________________
_______________________________________________________
IV. Anadzudzidwa ndi
Apolinto Pilato, anakhomedwa pa mtanda, nafa ndi kuikidwa m'manda, ndikukhala
ndi akufa.
1. Werengani za kugwidwa,
Kuyimbidwa mlandu, kukhomedwa pa mtanda ndi kuikidwa m'manda kwa Yesu mu
Yohane ndime 18 ndi19.
2. Werengani Mateyu
26:52-54 kuti mudziwe m'chifukwa chiyani Yesu sanachite chiri chonse.
3. Werengani Ahebri 2:14-17
kuti mumvetse chifukwa chake Yesu anayera Kufa.
4. Werengani m'bukhu la
Mateyu 27:45-46 ndi Luka 22:39-44 za m'mene Yesu anadzudzikira pototsedwa
ndipo Atate anamusiya yekha.
Mafunso:
1. Kodi Yesu anachimwa
chiyani? Nanga anadzudzikira chiyani? (Nanga ndi machimo andani amene
anadzudzikira?)
2. Werenganinso Yohane
12:27 kuti muone kudzipereka kwake. Nanga ndichifukwa chiyani anabwera pa
dziko lapansi?
3. Kodi womutsatira
Abulahamu anali ndani mu Ahebri 2:16 nanga m'chifukwa chiyani imfa inayeneleka?
4. Kodi zina kutotsedwa kwa
Yesu ndi ziti ndipo kufunika kwake ndikotani?
Mayankho:
1.
_____________________________________________________
_______________________________________________________
2.
_____________________________________________________
________________________________________________________
3.
_____________________________________________________
_______________________________________________________
4.
_____________________________________________________
_______________________________________________________
V. Tsiku latchitatu anauka
kwa akufa.
1. Werengani za kuuka kwa
Yesu mu Yohane 20.
2. Werengani za m'mene
Apositoli Paulo amanenera za kuuka kwa akufa mu Akorinto 15.
3. Werengani za m'mene
Akhrisitu adzakhalire ndi moyo mwa M'khrisitu.
4. Werengani za mphoto
yakupulumitsidwa m'mene Paulo anenera mu Akolose 3:1-4.
Mafunso:
1. Kodi Yesu anantsonyedza
bwanji kuti anali ndi mphamvu zogonjetsa imfa?
2. Kodi M'khrisitu
angakhale bwanji atauka mwa akufa?
3. Popeza anthu onse
kudzera mu machimo amangoganizira za kugahena, Vesi 5 likuthathauza chiyani
kwa inu?
4. Mwa anthu onse pa dziko
lapansi ndichifukwa chiyani Akhrisitu ayenera kukhala achitsangalaro?
Mayankho:
1.
_____________________________________________________
_______________________________________________________
2.
_____________________________________________________
________________________________________________________
3.
_____________________________________________________
_______________________________________________________
4.
_____________________________________________________
_______________________________________________________
VI. Anapita kumwamba,
nakakhala kudzanja lamanja la Mulungu Atate waphamvu zonse.
1. Werengani nkhani yopita
kumwamba m'mene iliri mu Macitidwe a Apositoli ndime 1:1-11.
2. Werengani kuti Yesu ali
kumwamba chifukwa cha ife mu
Ahebri 9:24-28.
3. Werengani Ahebri 4:14-16
kuti mudziwe chifukwa chake tili okhadzikika ndikukhala ndi moyo wabwino.
4. Werengani Yohane woyamba
2:1 kuti mumve zimene Yesu akuchita kumwamba.
5. Werengani Aefeso 2:1-9
kuti muone kuti moyo wathu ndi Yesu kumwamba ndi mphoto yapamwamba ndi
yamtengo wapatali.
Mafunso:
1. Kodi ndi ubatizo wanji
wa mzimu woyera umene Yesu analonjeza ophunzira ake, nanga unafanidziridwa
bwanji mu
Macitidwe 2:1-41?
2. Ndi chifukwa chiyani
pembedzo limodzi lokha linkakwanira?
3. Ndi chifukwa chiyani
tiyenera kukhala ndi chikhulupiliro m'maphephero anthu kwa Mulungu wamphamvu
zonse?
4. Kodi kukhala m'khrisitu
kumatanthauza kuti sitingachimwe?
5. Ganizirani ndime ya
Agalatiya 4:1-7. Kodi kusunga mwambo muulamuliro wamphamvu wonga ngati "Iwe
Pita" ndikosabvuta?
Mayankho:
1.
_____________________________________________________
____________________________________________________
2.
_____________________________________________________
________________________________________________________
3.
_____________________________________________________
_______________________________________________________
4.
_____________________________________________________
_______________________________________________________
5.
_____________________________________________________
_______________________________________________________
VII. Kuchokera kumwamba
adzabwera kudzaweruza amoyo ndi akufa.
1. Werengani Afilipi 3 kuti
mudziwe cholinga cha m'khrisitu aliyense.
2. Werengani Tito 2 za
m'mene m'khrisitu ayenera kukhalira poyembekezera kubwera kwa Yesu.
3. Werengani Atesalonika
woyamba 4:13-18 ndime imene imanena za kubwera kwa Yesu.
4. Werengani nthano zimene
Yesu ananena mu Mateyu 25.
5. Werengani Atesalonika
1:3-10 kuti muphunzire za chifundo cha Mulungu.
Mafunso:
1. Powerenga vesi 20 kodi
M'khrisitu angaganizire bwanji podzindikira kuti Yesu ndi Mlengi, Mpulumutsi,
ndi omuweludza wake?
2. Kodi dalitso la
chikhulupiliro cha M'khrisitu ndi chiyani?
3. Mu Chibvumbulutso 1:7
onani kusiyana kwa maganizo a onse amene adzaone kubwera kwa Yesu.
4. Kodi zofunikira zina
kuti Yesu atipulumutse ndi chiyani?
5. Poti anthu onse ndi
ochimwa ndipo ayenera kulangidwa, nanga Akhrisitu angapulumuke bwanji?
Mayankho:
1.
_____________________________________________________
____________________________________________________
2.
_____________________________________________________
________________________________________________________
3.
_____________________________________________________
_______________________________________________________
4.
_____________________________________________________
_______________________________________________________
5.
_____________________________________________________
_______________________________________________________
VIII. Ndikhulupilira mu
M'zimu Woyera.
1. Werenganinso Agalatiya
4:4-7 za m'mene mzimu unatsinthira akapolo atchimo kukhala ana a Mulungu.
2. Werengani Akorinto
wachiwiri 1:20-22 za njira za Mulungu kwa ana ake kuti akhalebe ndi
chikhulupiliro chawo.
3. Werengani Aefeso 1:13-14
m'mene Mulungu amakwanilitsira zofuna zathu kudzera mu m'zimu woyera.
4. Werengani Petro woyamba
1:1-2 m'mene Mulungu atsakhira ake.
Mafunso:
1. Kodi M'khrisitu
amapulumutsidwa kuchokera kuti? Nanga angapulumutsidwire kuti?
2. Tikawerenga Masalimo 1.
Kodi M'khrisitu ayenera kuchita chiyani pazofuna za mzimu woyera?
3. Kodi mzimu woyera
umatithandiza ife bwanji panopa ndi ku moyo wosatha?
4. Kodi Aroma 8:18-27
amanena bwanji za mzimu woyera m'mene umapulumutsira anthu osakhidwa?
Maynakho:
1.
_____________________________________________________
_______________________________________________________
2.
_____________________________________________________
________________________________________________________
3.
_____________________________________________________
_______________________________________________________
4.
_____________________________________________________
_______________________________________________________
IX. Ndikhulupilira
tchalichi cha akatolika oyera, ndichigwirizano cha angelo.
1. Werengani Genesesi 10
m'mene alotereza za tchalichi cha Akatolika kapena kunena kuti tchalichi cha
anthu onse.
2. Werengani Macitidwe 10
m'mene mungaphunzire kuti Yesu ndi Mfumu ya mafumu onse ndiponso kuti aliyense
angakakhale mu Ulemelero wa Mulungu osati Ayuda okha.
3. Werengani Akorinto
woyamba 12 zakuti tchalichi cha Yesu ndi chimodzi koma chiri ndi nthambi
zimbiri.
4. Werengani Aefeso 4:1-16
kuti muphuzire za thupi la Khrisitu likulira ndi kukhala ndi chikondi.
Mafunso:
1. Kodi M'chipangano
chakale anthu osakhidwa ali ndani?
2. Kodi Genesesi
amakwanilitsidwa bwanji mu Macitidwe 10?
3. Kodi mphoto
zosiyanasiyana zingatsangalatse bwanji m'chiyanjano cha angelo ku ulemero wa
Mulungu?
4. Kodi m'chifukwa chiyani
umodzi mu thupi la Khrisitu ndi wofunikira kwambiri ngati cholinga cha
M'khrisitu aliyense ndi kupembeza Mulungu?
Mayankho:
1.
_____________________________________________________
_______________________________________________________
2.
_____________________________________________________
________________________________________________________
3.
_____________________________________________________
_______________________________________________________
4.
_____________________________________________________
_______________________________________________________
X. Kukhulukiridwa kwa
machimo.
1. Werengani Yohane woyamba
1:7 ndi Yohane woyamba 2:1-2 kuti mudziwe zimene zinachitika pamene Akhrisitu
anagwera mu machimo.
2. Werengani Aroma 7:21-25
kuti olo m'Khrisitu wopulumutsidwa ayenera kugonjetsa machimo a padziko
lapansi.
3. Werengani Aroma 3:21-28,
Agalatiya 2:15-16 ndi Ahebri 11 m'mene timaphunzira kuti timayesedwa kudzera
m'chikhulupiliro cha chisomo cha Mulungu osati m'chifuniro chathu.
4. Werengani Mika 7:18-19
kuti mumve m'mene chikhulukiliro chathu chinayanjatsilidwa Yesu asanabadwe.
Mafunso:
1. Kodi tingapulumitsidwe
bwanji?
2. Chifukwa chiyani
m'Khrisitu aliyense ayenera kupepha kukhululukilidwa kwa machimo tsiku liri
lonse?
3. Ndi m'njira yotani
machimo amachoka mwa munthu wochimwa ngati ine ndi kukhala m'Khrisitu wopanda
tchimo?
4. Kodi muganiza bwanji za
chigwirzano cha chipangano chakale ndi chatsopano?
Mayankho:
1.
_____________________________________________________
____________________________________________________
2.
_____________________________________________________
________________________________________________________
3.
_____________________________________________________
_______________________________________________________
4.
_____________________________________________________
_______________________________________________________
5.
_____________________________________________________
_______________________________________________________
XI. Kuuka kwa akufa.
1. Werengani Luka 16:19-31
m'mene Yesu ananenera zina za moyo wosatha.
2. Werengani Afilipi
1:21-24 kuti mudziwe m'mene Paulo anaganidzira za moyo ndi imfa.
3. Werengani Chibvulutso
20:11-15 kuti muone m'mene tidzaweluzidwire.
4. Werengani Yohane woyamba
3:1-3 zakusiyana kokhala m'Khrisitu ndio kusakhala m'Khrisitu.
5. Werengani Akorinto
woyamba 2:6-9 kuti umdziwe za zimene anankhozela m'Khrisitu aliyense.
Mafunso:
1. M'mene nthano yi
ikunenera kodi tidzakhala ndi chifundo kapena chisoni ndi anzathu okonda za
dziko lapansi?
2. Kodi m'khrisitu
nagachite chiyani kuti asiye kukonda moyo wa dziko lapansi ndi kukalowa ku
moyo wosatha?
3. Werengani Masalimo 139.
Kodi timakhala ndi mtendere kapena dadaulo podziwa kuti Mulungu amadziwa
maganiza ndi zochita zathu.
4. Chifukwa chiyani anthu
ena samalapa machimo awo ndi kubwera kwa Yesu kuti awakhululukire?
5. Kodi ulemelero
wakumwamba ndikukhala ndi Mulungu?
Mayankho:
1.
_____________________________________________________
_______________________________________________________
2.
_____________________________________________________
________________________________________________________
3.
_____________________________________________________
_______________________________________________________
4.
_____________________________________________________
_______________________________________________________
XII. Ndikukhala ndi moyo
wosatha. Amen.
1. Werengani Akorinto
wachiwiri 5:1-6 kuti mumve za nyumba yathu ya kumwamba.
2. Werengani Chibvumbulutso
22 ndipo mumalingaliro anu onse muone zimene anatikhozera.
3. Werengani Mateyu 6:9-13
m'mene Yesu anaphunzitsa ophunzira ake kupephera.
4. Werengani Akorinto
wachiwiri 1:18-20 ndi
Chibvumbulutso 22:21-22 za
m'mene liwu loti "Amen" limagwiritsilidwa ntchito.
Mafunso:
1. Kodi moyo wathu ndi
wokonda dziko lapansi ndi katundu?
2. Kodi ganizo ndi
chinthunzi cha nyumba yathu ya kumwamba chimatithandiza bwanji za moyo wathu
wa padziko lapansi?
3. Muphephero lomwe Yesu
anaphunzitsa, analangiza kuti Dzina la Atate lilemekedzedwe ndi zofuna zake
zichitike zimakuthandizani kuona za nyumba ya Atate kumwamba?
4. Poti Ame pachiyambi
ankatathauza Choonadi, Kukhulupilika, ndi chiyembekezo, nanga umboni wa Yohane
mu Cibvumbulutso ndi wotani kwa ife nanga umatithandiza bwanji?
Mayankho:
1.
_____________________________________________________
_______________________________________________________
2.
_____________________________________________________
________________________________________________________
3.
_____________________________________________________
_______________________________________________________
4.
_____________________________________________________
_______________________________________________________
Cholinga
Cholinga cha bukhuli
ndikuthandiza anthu kuti aphunzire Baibulo pamodzi. Mu Mateyu 18:19-20 Yesu
anati, "ndinenanso, ngati awiri a inu mugwirizana pa zofuna zanu, Atate
akumwamba azakuchitirani. Poti ndimakhala pomwe pali anthu awiri kapena atatu
mudzina langa."
Muli ololedwa kulemba
bukuli kachiwiri. Ngati mufuna kulemba mchinenero china, chonde lemberani
kwa: Les Hendricks, c/o Christian Hope Association, 205 South BC Avenue, Suite
#105, Lynden WA 98264, USA. Tizakuthandizani kulemba bukhuli kwa ulere. Tiyeni "Aliyense wa ife
aphunzitse mzake" chikhale cholinga chathu ndipo "Ulemelero wa
Mulungu" ukhale chofuna chathu.
Choncho . . .
Mwamaliza kuphunzira mau a
Mulungu, mungathe kuziyetsa nokha? Kodi ubwenzi wanu ndi Yesu Khrisitu ndi
wotani? Ngati m'mene Timoteo wachiwiri 3:14-17 alembera zakufunikira kwa mau a
Mulungu mu njira zosiyanasiyana, koma Yakobo amanenanso kuti kudziwa mau a
Mulungu kokha sikutathauza chipulumutso.
Kuti munthu akhale mwana
wa Mulungu, ayenera kuchita ndi kudziwa izi:
1. Kudziwa zotsatira za
machimo. Werengani Luka 18:9-14; Samueli wachiwiri ndime 11 ndi 12:1-13;
Aroma 3:10-12.
2. Kulandira chipulumutso.
Werengani Aefeso 2:1-9; Mariko 16:16; Yohane 20:24-28.
3. Kufalitsa uthenga ndi
ntchito zabwino. Werengani Mateyu 10:32-33; Luka 23:39-43; Yakobo 2:26;
Yesaya 6:8.
Werengani ndi kuganizira
mozama za mau ndi ndimezi ndipo pepherani polapa machimo, ndikupepha Yesu kuti
akhale mpulumutsi ndi mtsogoleri wa moyo wanu. |